Hadith Collection - Into Chichewa
Ndine (translator) M'bale wanu Abuwbakr Size, Zikomo
'Umar (Mulungu asangalale naye) adati: Mtumiki ﷺ adanena kuti,
"Usiku wathawu wina wake, wochokera kwa Ambuye wanga, anadza kwaine (mkulota) pomwe ndinali mu (chigwa cha) 'Aqiq nati kwa ine, "Pemphera (swalah) mu chigwa ichi chodalitsika ndipo unene: "Labbaik" pa 'Umra ndi Hajj."
أَنَّ عُمَرَ ـ رضى الله عنه ـ حَدَّثَهُ قَالَ حَدَّثَنِي النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم قَالَ " أَتَانِي اللَّيْلَةَ آتٍ مِنْ رَبِّي وَهْوَ بِالْعَقِيقِ أَنْ صَلِّ فِي هَذَا الْوَادِي الْمُبَارَكِ وَقُلْ عُمْرَةٌ وَحَجَّةٌ " (وَقَالَ هَارُونُ بْنُ إِسْمَاعِيلَ حَدَّثَنَا عَلِيٌّ عُمْرَةٌ فِي حَجَّةٍ. )
Sahih al-Bukhari, 7343
Vol. 9, Book 92, Hadith 442
Book of holding fast to the
Abu Burda (Mulungu asangalale naye) adati,
"Pamene ndinafika ku Madina, 'Abdullah bin Salam anakumana nane ndipo anati kwa ine, "Nditsateni kunyumba yanga kuti ndikakupangileni chakumwa mu kapu imene Mtumiki ﷺ ankamwera, ndikutinso ukapemphere Swalah mu mzikiti umene Mtumiki ﷺ anali kupemphera."
Choncho ndinapita naye (limodzi), ndipo anandimwetsa Sawiq ndikundipatsa tende kuti ndidye. Ndipo kenako ndinadzapemphera mu mzikiti wake (umene Mtumiki ﷺ anapemphereramo).
عَنْ أَبِي بُرْدَةَ، قَالَ قَدِمْتُ الْمَدِينَةَ فَلَقِيَنِي عَبْدُ اللَّهِ بْنُ سَلاَمٍ فَقَالَ لِي انْطَلِقْ إِلَى الْمَنْزِلِ فَأَسْقِيَكَ فِي قَدَحٍ شَرِبَ فِيهِ رَسُولُ اللَّهِ صلى الله عليه وسلم، وَتُصَلِّي فِي مَسْجِدٍ صَلَّى فِيهِ النَّبِيُّ صلى الله عليه وسلم. فَانْطَلَقْتُ مَعَهُ، فَسَقَانِي سَوِيقًا، وَأَطْعَمَنِي تَمْرًا، وَصَلَّيْتُ فِي مَسْجِدِهِ."
Sahih al-Bukhari, 7342
Vol. 9, Book 92, Hadith 441
Book of holding fast to the
Click here to claim your Sponsored Listing.
Category
Website
Address
Pretoria